Kupeza Choonadi

Phunziro 10

KUPEMBEZA: Kutamanda Yehova m'busa wathu

Masalimo 23: 1-6

KUWERENGA MAWU

Kuwerenga ndi kumvetsera mawu. Kubwereza kuwerenga ndi kumvetsera mawu mpaka aliyense atamvetsetsa.

x1.0
  23:1Yehova ndiye mʼbusa wanga, sindidzasowa kanthu.
    2Amandigoneka pa msipu wobiriwira,
  amanditsogolera ku madzi akumwa abwino,
    3amatsitsimutsa moyo wanga.
  Amanditsogolera mʼnjira zachilungamo
    chifukwa cha dzina lake.
  4Ngakhale ndiyende
    mʼchigwa cha mdima wakuda bii,
  sindidzaopa choyipa,
    pakuti Inu muli ndi ine;
  chibonga chanu ndi ndodo yanu
    zimanditonthoza.

  5Mumandikonzera chakudya
    adani anga akuona.
  Mumadzoza mutu wanga ndi mafuta;
    chikho changa chimasefukira.
  6Zoonadi, zokoma ndi chikondi chosasinthika zidzanditsata
    masiku onse a moyo wanga,
  ndipo ndidzakhala mʼNyumba ya Yehova
    kwamuyaya.

KUFOTOKOZERA

Kufunsa aliyense afotokozere m'mene wamvera mawuwo

ZOYENERA KULINGALIRA


Get it on Google Play
Download on the App Store

Get Discovery Bible Studies on your phone

Discover copyright ©2015-2026 discoverapp.org

Chichewa scriptures from Biblica® Tsekulani Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero™. Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc. All rights reserved